Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Bambo wazaka 70 akhala kundende zaka 14 chifukwa chogwililira

Bwalo lamilandu ku Balaka lalamula a Phutheya Galeta azaka 70 kuti akagwire ndende yakalavula gaga kwa zaka 14 chifukwa chochita zadama ndi mwana.

Ofalitsa nkhani za Polisi ya Balaka Gladson M’bumpha watsimikiza nkhaniyi ndipo wati a Galeta adagwilira mwanayo yemwe ndi wazaka 14 mwezi wa June,2024.

Oweluza milandu Joshua Nkhono wati wapereka chilangocho kuti ena atengerepo phunziro.

A Galeta amachokela mmudzi wa Malula kwa mfumu yaikulu Sawali ku Balaka.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Boma layamikira ntchito za NASCENT Solutions polimbikitsa maphunziro

Austin Fukula

Akatswiri ovina nyimbo za soja akhetsa misozi

Emmanuel Chikonso

Salima Sugar ikupereka K500 million kwa osamuka m’minda yawo

Foster Maulidi
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.