Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Nkhani

Watentha mwana wake chifukwa cha mbatata

Apolisi ku Dowa amanga mayi wazaka 35 chifukwa chomuganizira kuti wavulaza mwana wake wa zaka 12 ndi madzi otentha, mwanayo atadya mbatata asanapemphe mayi akewo.

Ofalitsankhani zapolisi ku Dowa, Alice Sitima, wati mayiyo, Chimwemwe Kayere, anachoka mammawa kupita kumunda ndi mwamuna wake kusiya mwanayo akugona.

Mwanayo atadzuka, anaphika mbatata yomwe inali mnyumbamo kuti adye.

Koma mayiyo atabwera kuchokera kumundako, sizinamusangalatse ndipo anaphula pamoto poto yemwe munali mbatatayo ndikumuthira mwanayo, iye ndikuthawa.

Bambo amwanayo atafika anamutenga ndikuthamangira naye kuchipatala.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Two brothers nabbed over possessing Cannabis without permit

Romeo Umali

Questions over authenticity of Bushiri’s extradition request

Olive Phiri

MEC yapempha anthu akalembetse mu kaundula wa chisankho cha makhansala

Arthur Chokhotho
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.