Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Apereka njinga zamoto zothandizira ntchito zaumoyo

Bungwe la Malawi Network of People Living with HIV and AIDS (MANET+) lapereka njinga yamoto ku ofesi ya zaumoyo ya Mzimba North yomwe ithandizire pantchito za umoyo m’bomali.

Mkulu wa bungweli, a Lawrence Khonyongwa ati njingayi ndi gawo la ntchito yaikulu yotukula zaumoyo yomwe ikulandira thandizo kuchokera kuthumba la Global Fund.

“Ili ndi gawo la chitatu la ntchito yotchedwa COVID-19 Response Mechanism yomwe cholinga chake ndikuyika dongosolo lokonzekera mavuto ena aliwonse omwe angagwe mwadzidzidzi,” anatero a Khonyongwa.

Iwo anati matenda a COVID 19 anapereka maphunziro osiyanasiyana ndikuti limodzi mwamaphuzirowa ndikukhala okonzeka.

A Khonyongwa anati njingazi azigawanso mmaboma a Likoma, Rumphi komanso Nkhotakota.

 

Olemba Henry Haukeya

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NYCOM receives budget boost for youth empowerment programmes

MBC Online

UNAIDS HAIL CHAKWERA’S ADMINISTRATION IN FIGHTING HIV/AIDS

McDonald Chiwayula

HRCC salutes Kasambara’s legacy

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.