Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Apereka njinga zamoto zothandizira ntchito zaumoyo

Bungwe la Malawi Network of People Living with HIV and AIDS (MANET+) lapereka njinga yamoto ku ofesi ya zaumoyo ya Mzimba North yomwe ithandizire pantchito za umoyo m’bomali.

Mkulu wa bungweli, a Lawrence Khonyongwa ati njingayi ndi gawo la ntchito yaikulu yotukula zaumoyo yomwe ikulandira thandizo kuchokera kuthumba la Global Fund.

“Ili ndi gawo la chitatu la ntchito yotchedwa COVID-19 Response Mechanism yomwe cholinga chake ndikuyika dongosolo lokonzekera mavuto ena aliwonse omwe angagwe mwadzidzidzi,” anatero a Khonyongwa.

Iwo anati matenda a COVID 19 anapereka maphunziro osiyanasiyana ndikuti limodzi mwamaphuzirowa ndikukhala okonzeka.

A Khonyongwa anati njingazi azigawanso mmaboma a Likoma, Rumphi komanso Nkhotakota.

 

Olemba Henry Haukeya

Related posts

MEC impressed by progress of 3rd phase voter registration

Romeo Umali

US Govt to assist Malawi after disaster declaration

Romeo Umali

RBM Introduces 50, 20 Kwacha coins

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.