Mwambo wa maliro a malemu Hope Chisanu watsala pang’ono kuyamba m’mudzi wa Nyaka, mdera la mfumu yayikulu Kalumbu, m’boma la Lilongwe.
A Chisanu adamwalira pa 1 June m’dziko la USA kumene amakhala ndipo thupi lawo lafika m’dziko muno lachiwiri lapitali.
Iwo adagwirapo ntchito ku wayilesi ya Malawi Broadcasting Corporation (MBC) kumene adatchuka ndi dzina lakuti ‘Uncle Bembelezi’ ndipo adadziwikanso ndi zisudzo akamachita sewero ndi gulu la Wakhumbata Ensemble Theatre.
Iwo amachita nawo sewero la Theatre of the Air lomwe limawuluka pa wailesi ya MBC Radio 1.
Olemba: Isaac Jali