Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Alimi aguliretu mbewu zoyenera — SeedCo

Kampani yopanga mbewu ya SeedCo yalangiza alimi kuti aguliretu mbewu zovomerezeka nyengo ya dzinja isanafike.

A Dennis Mdzalimbo, omwe amaona zamalonda  Ku kampaniyi  anati kugula mbewu zovomerezeka kumathandiza kuti ulimi ukhale waphindu.

Iwo amayankhula izi pa msonkhano omwe anachititsa ndi anthu komanso makampani omwe amagulitsa mbewu ochokera ku chigawo cha kumpoto.

A Mdzalimbo alangizanso alimi kuti adzitsatira ulangizi wa zanyengo kuti adzibzyala mbewu zogwirizana ndi momwe mvula ikugwera.

Malingana ndi akatswiri a zanyengo, madera ena m’chigawo cha kumpoto mugwa mvula yocheperako chaka chino kamba ka mphepo yotchedwa La Nina.

 

Olemba: Chimwemwe Milulu

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NGO drills 500 boreholes in the Southern Region

Jeffrey Chinawa

UNECA hails Malawi’s PPP investment

Tasungana Kazembe

CHAKWERA CALLS FOR HARD WORK AMONG MALAWIANS

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.