Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Adzudzula mmodzi mwa atsogoleri a DPP kaamba kolankhula moopseza

Bungwe la Civil Society Elections Integrity Forum ladzudzula mmodzi mwa atsogoleri a chipani cha Democratic Progressive (DPP) a Norman Chisale kaamba ka mchitidwe olankhula mau owoopseza komanso aukali pomwe akupangitsa misonkhano.

Mkulu wa bungweli a Benedicto Kondowe ati malankhulidwe woterewa akhoza kudzagwetsa mphwayi anthu omwe akufuna kudzaponya voti pachisankho chomwe chichitike pa 16 September chaka chino.

A Kondowe anatinso powonjezera kudzetsa mantha, izi zikhoza kudzabweretsa ziwawa.

Mwazina, a Chisale, omwe ndi mkulu owona za achinyamata mchipani cha DPP, akhala akumayankhula kuti mukuona kwawo,mavoti akhoza kudzaberedwa ndipo nawonso ali ndikuthekera kobera chisankho.

Iwo akhalanso akutchula atsogoleri ena andale maina monga a Khakhakha pongotchulapo ena.

Pakadali pano, mneneri wachipani cha DPP a Shadreck Namalomba ati malankhulidwe oterewa samayimira chipani chawo kotero izi ndi zosavomerezeka konse.

A Namalomba anawonjezeranso kunena kuti atsogoleri onse andale ayenera kupewa kulankhula mawu onyoza komanso oopseza ndipo mmalo mwake ayenera kufotokoza mfundo zomwe zikhonza kukopa anthu.

 

Olemba: Timothy Kateta

Related posts

Religious leaders urged to embrace Malawi 2063

Romeo Umali

Malawi Red Cross calls for responsible reporting during disasters

Rabson Kondowe

K22M clinic opened in Mzuzu

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.