Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Abusa asiye kudalira nkhosa zawo pachuma

Kampani ya Synthesis Agriculture yalangiza  abusa ena kuti asiye kudalira nkhosa zawo pa umoyo wawo wa tsiku ndi tsiku ndipo m’malo mwake ayambe kugwira ntchito zaulimi kuti azidzithandiza okha.

M’modzi mwa akuluakulu ku kampaniyi a Aaron Chitimbe wati nthawi yakwana  yoti abusa ayambe kudzidalira  pachuma.

Iwo ati pamene abusa akuwuza anthu kuti adzapita kumwamba akuyenera kudziwanso kuti asananyamuke ulendo wakumwamba akuyenera kuti akhale ndi chakudya padziko lapansi  pompano.

A Chitimbe alankhula izi pamaphunziro omwe cholinga chake ndikulimbikitsa abusa ubwino wochita ulimi pamene akukonzekera kupuma pantchito omwe akuchitikira mu mzinda wa Blantyre.

Maphunzirowa abweretsa pamodzi atumiki a Mulungu ochokera m’maboma osiyanasiyana chigawo cha kum’mwera.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

SCT gives hope to Cyclone Freddy survivors in Nsanje

MBC Online

MUST needs K2 billion to complete lab construction

MBC Online

Crowds gather at Chileka Airport to welcome Chakwera

Secret Segula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.