Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani

Majaji agwidwa ndi chisoni ndi imfa ya Kasambara

Majaji m’dziko muno ati ali ndi chisoni kaamba ka imfa ya a Raphael Kasambara omwe anali katswiri wa za malamulo komanso yemwe anathandiza kwambiri polimbikitsa ntchito zamalamulo m’dziko muno.

Justice Zione Ntaba, anena izi pamwambo otsanzikana ndi a Kasambara omwe ukuchitikira kunyumba kwa malemuwa ku Nyambadwe mu mzinda wa Blantyre.

Posachedwapa, maliro apita nawo ku CI komwe kukachitikire mapemphero asananyamule thupi la Malemuwa pa ndege kupita kumudzi kwawo m’boma la Nkhata Bay komwe akaliyike m’manda lolemba.

A Michael Usi, nduna yazosamalira chilengedwe, ndiwo akuimira boma pa mwambowu.

 

Related posts

First Lady urges women to lead in praying for Malawi’s progress

Alinafe Mlamba

Zavutaso ku COSAFA

Romeo Umali

Bullets look to seal the deal against Arrows

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.