Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

UTM yalimbikitsa achinyamata

Chipani cha UTM chalimbikitsa achinyamata kuti alembetse mu kaundula wa unzika kuti adzakhale ndi mwai oponya nawo voti  pachisankho chachikulu chomwe chichitike mdziko muno chaka cha mawa.

Mkulu wa achinyamata mu chipanichi a Penjani Kalua amalankhula izi ku Mangochi pa mwambo okweza mbendera ya chipanichi.

Chipani cha UTM akuti chinatsitsa mbendera yake mwezi wa June potsatira imfa ya mtsogoleri wake yemwenso anali wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Dr Saulos Chilima.

“Tikupempha achinyamata onse omwe akufuna kudzaponya nawo voti  kuti asachite ulesi olembetsa mkaundula wa chiphaso cha unzika ngati akufuna kudzaponya nawo voti mwezi wa September chaka cha mawa,” anatero a Kalua.

 

Olemba: Owen Mavula

Related posts

Parliament passes Appropriation Bill for additional K570BN in just ended 2023/24 Fiscal Year

Romeo Umali

‘Government is trying to restore, protect natural resources’

Romeo Umali

IT firm touts AI-driven financial inclusion

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.