Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

UNICEF ipitiliza kuthandiza Mtukula Pakhomo

Bungwe la UNICEF lati ndilokondwa ndi momwe ntchito za ‘Mtukula Pakhomo’ zikuthandizira kuchepetsa umphawi mmakomo ambiri mdziko muno.

Yemwe akuyimira bungweli kuno ku Malawi a Shadrack Omol ayankhula izi pomwe amawonelera ntchito yolemba anthu ena omwe akulowa nawo mundandanda olandira ‘Mtukula Pakhomo’ ku Doroba kwa mfumu yaikulu Ntwalo ku Mzimba.

Iwo ati bungwe lawo lipitiriza kupereka thandizo kuntchitoyi ati chifukwa anthu ambiri akupindula ndi ntchitoyi.

Mmodzi wa akuluakulu ku unduna owona zosamalira anthu a Laurent Kansinjiro ayamikira bungwe la UNICEF chifukwa linayamba kuthandiza ntchito ya ‘Mtukula Pakhomo’ m’chaka cha 2006 pomwe ntchitoyi inkayamba.

Padakali pano anthu oposa 1,500,000 ndiomwe akulandira ‘Mtukula Pakhomo’ mdziko muno.

Wolemba: Henry Haukeya

Related posts

Bus ya Bullets inakalibe mmanja mwa khothi

Rabson Kondowe

NRB yalemba anthu opyola 12 million

Alinafe Mlamba

MAIIC yapanga phindu lokwana K2.5 billion mu 2023

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.