Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

UNICEF ipitiliza kuthandiza Mtukula Pakhomo

Bungwe la UNICEF lati ndilokondwa ndi momwe ntchito za ‘Mtukula Pakhomo’ zikuthandizira kuchepetsa umphawi mmakomo ambiri mdziko muno.

Yemwe akuyimira bungweli kuno ku Malawi a Shadrack Omol ayankhula izi pomwe amawonelera ntchito yolemba anthu ena omwe akulowa nawo mundandanda olandira ‘Mtukula Pakhomo’ ku Doroba kwa mfumu yaikulu Ntwalo ku Mzimba.

Iwo ati bungwe lawo lipitiriza kupereka thandizo kuntchitoyi ati chifukwa anthu ambiri akupindula ndi ntchitoyi.

Mmodzi wa akuluakulu ku unduna owona zosamalira anthu a Laurent Kansinjiro ayamikira bungwe la UNICEF chifukwa linayamba kuthandiza ntchito ya ‘Mtukula Pakhomo’ m’chaka cha 2006 pomwe ntchitoyi inkayamba.

Padakali pano anthu oposa 1,500,000 ndiomwe akulandira ‘Mtukula Pakhomo’ mdziko muno.

Wolemba: Henry Haukeya

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Mphunzitsi ali mchitokosi atagwilira mwana

Davie Umar

Ntchito za GESD zakondweretsa anthu m’boma la Chiradzulu

MBC Online

M’busa Kawinga apereka K25 million kwa ana amasiye

Yamikani Simutowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.