Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Bus ya Bullets inakalibe mmanja mwa khothi

Bus ya FCB Nyasa Big Bullets sinabwerere kuma ofesi atimuyi, dzulo italandidwa ndi ma Sherrif.

Bus-yi inalandidwa kaamba koti timuyi inali ndi ngongole ya ndalama zokwana K25 million ndi mphunzitsi wawo wakale Franco Ndawa.

Malingana ndi modzi mwa akuluakulu a Bullets, a Albert Chigoga, timuyi yalipira ndalamayi kuphatikizapo K4 million ndipo akudikira ndondomeko zokhudza malamulo kuti bus-yi ibwerere zomwe akuyendetsa ndi owayimira pamilandu.

Chigoga watsutsaso kuti timuyi ili ndi malingaliro ochotsa osewera ena pazifukwa kuti akupangila dala kuti timuyi isamachite bwino.

Lachiwiri, osewera a Bullets anakana kuchita zokonzekera za timuyi.

 

By Praise Majawa

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Chakwera heads to Southern Region for official duties

MBC Online

13th Smart Africa meeting underway in Lilongwe

Yamikani Simutowe

Chakwera wanyamuka kubwelera ku Lilongwe

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.