Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Scorchers lero imwemwetera

Atsikana amene amasewera mpira wamiyendo mu timu yadziko lino ya Scorchers adzuka ndinkhope zowala chifukwa lero boma likuyembekezeka kukwaniritsa zimene mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, analonjeza kuti apatsidwa malo chifukwa chotenga chikho cha COSAFA m’dziko la South Africa.

Unduna wa za malo ukuyembekezeka kugawa malo kwa aliyense wa osewerawa, ndipo malowa ndi okula milingo 35 mulitali ndi milingo 25 mulifupi ku Area 45 mu mzinda wa Lilongwe.

Malinga ndi akuluakulu ku unduna wa za masewero, ntchitoyi ikuyembekezeka kuyamba mma 8:30 mmawa uno.

Related posts

Mponda chinsinsi chake ndi Maonga

Romeo Umali

Dziko la Malawi tsopano liri ndi mtsogoleri wa masomphenya – Mkaka

Alinafe Mlamba

Anthu akukhamukira kumwambo wa Chikumbutso ku Mulanje

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.