Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Zonse zili mchimake, yatero PP

Nthumwi 1,100 zochekera mzigawo zonse za dziko lino za chipani cha People’s zikuyembekeza kusankha atsogoleri atsopano a chipanichi pa msonkhano waukulu wa chipanichi, umene uyambe masana ano munzinda wa Lilongwe.

Padakali pano, nthumwi zikulowa mchipinda momwe muchitikire msonkhano umenewu.

Wapampando wa komiti yomwe yakonza msokhanowu, a Peter Kamange, wati maina a omwe apikisane pa maudindo osiyanasiyana awatulutsa masana ano.

“Tikutsirizitsa ntchito younika maina a omwe apikisane. Anthu angapo apereka zikalata zoti apikisane pa udindo wa mtsogoleri wa People’s kotero tikatsiriza kuunika zipepala zomwe anthu apereka, titulutsa mndandanda wonse kuti anthu onse adziwe,” atero a Kamange.

Iwo ati zonse zili mchimake, ndipo akuyembekezera kuti msonkhanowu, umene uthe mawa loweruka, uyenda bwino.

Mutu wa msonkhanowu ndi ‘Restoring the Hope: Building a Brighter Future Together’.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

We got you covered — NEEF

MBC Online

MBC gets its turn at Parliament

Trust Ofesi

Bus company’s innovation excites African media in China

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.