Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Zonse zili mchimake, yatero PP

Nthumwi 1,100 zochekera mzigawo zonse za dziko lino za chipani cha People’s zikuyembekeza kusankha atsogoleri atsopano a chipanichi pa msonkhano waukulu wa chipanichi, umene uyambe masana ano munzinda wa Lilongwe.

Padakali pano, nthumwi zikulowa mchipinda momwe muchitikire msonkhano umenewu.

Wapampando wa komiti yomwe yakonza msokhanowu, a Peter Kamange, wati maina a omwe apikisane pa maudindo osiyanasiyana awatulutsa masana ano.

“Tikutsirizitsa ntchito younika maina a omwe apikisane. Anthu angapo apereka zikalata zoti apikisane pa udindo wa mtsogoleri wa People’s kotero tikatsiriza kuunika zipepala zomwe anthu apereka, titulutsa mndandanda wonse kuti anthu onse adziwe,” atero a Kamange.

Iwo ati zonse zili mchimake, ndipo akuyembekezera kuti msonkhanowu, umene uthe mawa loweruka, uyenda bwino.

Mutu wa msonkhanowu ndi ‘Restoring the Hope: Building a Brighter Future Together’.

 

Related posts

BROADCASTERS CHALLENGED TO PRODUCE MESSAGES OF HOPE

MBC Online

Norway, WFP sign MOU for $5.2million support towards El Niño response efforts

Rabson Kondowe

Chitipa takes crime fight head-on

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.