Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Zokonzekera zamwambo wa MBC Zokonda Amayi zili mchimake

Wapampando wamwambo wa MBC Zokonda Amayi wa chaka chino, mayi Mervis Senga, ati zonse zokonzekera zamwambo wa Zokonda Amayi Macheza umene uchitikire munzinda wa Mzuzu zili mchimake.

Mayi wafuko lino, Madam Monica Chakwera, ndi amene akuyembekezeka kukhala mlendo olemekezeka pamwambowo.

A Senga ati padakali pano amayi oposa 400 kuchoka muzigawo zonse zadziko lino ndiamene afika kale kudzakhala nawo kumwambo okondwelera tsiku la anakubala kudzera mu pologalamu ya Zokonda Amayi wu mawa lino.

A Senga, omwenso ndiogwilizira udindo wa mkulu oyang’anira nkhani ku MBC, adatinso ndipofunika kuti amayi akhale ndimaphunziro osiyanasiyana monga a zamalonda ndi zaumoyo.

 

Olemba: Chisomo Manda

Related posts

Lucius anali bwenzi lama Rasta — Ras Jonah

Romeo Umali

K22M clinic opened in Mzuzu

Rabson Kondowe

Ansah wants speedy development of Nacala Corridor

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.