Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Tisunge bata’

Senior Chief Inkosi Champiti ya m’boma la Ntcheu yapempha anthu m’dziko muno komanso angoni kuti asunge bata ndi mtendere pamene lero kuli mwambo woyika m’manda malemu Dr Saulos Chilima, wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino.

Iwo ati angoni ndi anthu a mtendere choncho sakufuna kumva za ziwawa zina zili zonse.

“Malemu Dr Chilima, a Bhiyeni, anali munthu wokonda mtendere choncho sitikufuna kumva zoipa zina zilizonse, angoni sayenela kugenda,” anatero Senior Chief Champiti.

Mwa zina, mfumuyi yati anthu asade nkhawa ndipo afike kudzapereka ulemu wawo otsiriza chifukwa akhazikitsa chitetezo chokwanira ngati mafumu pamodzi ndi apolisi.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Solar energy still a solution to transform agriculture — PDU

Beatrice Mwape

MHRC for legal action over infant’s death at Mzimba Checkpoint

MBC Online

Gulu la alimi lapeza K620 million kudzera mu ulimi wa nzimbe

Doreen Sonani
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.