Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Politics

Sitisankha opambana chisankho — MEC

Bungwe loona zisankho m’dziko muno la MEC lati opikisana pa chisankho amaoneka papepala loponyera voti potengera zilembo zoyambilira za maina awo osati chipani chomwe akuyimira pa chisankho.

Pa chifukwa ichi, bungweli latsutsa zomwe ena akunena kuti lasankha munthu wina komanso likufuna kuti munthu yemwe akuyimira chipani china adzapambane pa chisankho chapadera cha khansala m’dera la Mwansa m’boma la Mangochi.

Bungweli lichititsa chisankho chapadera ku Mwansa pa 23 mwezi uno.

Chikalata chomwe MEC yatulutsa ndipo wasayinira ndi mkulu ofalitsa nkhani za bungweli a Sangwani Mwafulirwa chapempha omwe akupikisana pa chisankhochi, zipani zandale ndi ozitsatira kuti atsatire malamulo a chisankho omwe anasayinira.

A Mwafulirwa ati “Atsogoleri a zipani akupemphedwa kukopa anthu powauza mfundo zomveka osati kumawauza zinthu zabodza”.

Bungweli lakumbutsa anthu kuti silitumikira chipani chilichonse koma ntchito yake ndi kuchititsa chisankho mokomera anthu onse.

Olemba: Kondwani Chinele

Related posts

ActionAid hands 12 motorcycles to health project partners

Rabson Kondowe

Mabedi confident of his charges

Rabson Kondowe

Lapukeni laid to rest in Mangochi

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.