Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani

Ochita malonda athandiza ana asukulu

Ochita malonda pa msika wa Nsungwi ku Area 25 m’mzinda wa Lilongwe, a Emmanuel Pensulo, apereka unifolomu kwa ophunzira khumi apa sukulu ya Kalambo.

A Pensulo anati unifolomu ndi yofunika chifukwa ana amadziwika komanso kuti ana saonekera kuti akuchokera ku banja losowa chifukwa onse amavala mofanana.

Iwo anati ndi khumbo lawo kufikira ana oposa 1000 m’boma la Lilongwe ndi thandizo lomweli.

Wachiwiri kwa mphunzitsi wa mkulu pa sukuluyi, a Frotrida Kumwenda Nzimba, anati thandizoli lafika mu nthawi yake pamene ana ambiri akulephera kupita ku sukulu kaamba kosowa unifolomu.

A Nzimba anapemphanso anthu ena ofuna kwabwino kuti achitenso moteremu.

Related posts

PRESIDENT CHAKWERA COMMENDS CYCLONE FREDDY SURVIVORS FOR BEING RESILIENT

MBC Online

Mulhakho wa Alhomwe to elect new members on 2 March

Romeo Umali

Mthunzi Funeral Services open new centre in Lilongwe

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.