Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Nyasulu ndi mfumu yatsopano ya mnzinda wa Mzuzu

A Kondwani Nyasulu awasankha kukhala mfumu ya mnzinda wa Mzuzu pazisankho zomwe zikuchitika mu mzindawu zosankha mfumuyi komanso wachiwiri wake.

A Nyasulu, amene ndi a chipani cha UTM, awasankha atapeza mavoti asanu ndi anayi pomwe a Desire Nyirenda a MCP apeza mavoti asanu ndi awiri.

Anthu omwe akuponya votiyi alipo 16.

Zisankhozi anayamba aziyimitsa kamba koti khansala Pillie Chiumia wadera la kuzambwe kwa Mchengautuba mu mzindawu anadandaula kuti a Nyirenda si oyenera kuima nawo kamba koti akuyankha mlandu ku khoti woganiziridwa kuti anagonana ndi mwana wachichepere.

Izi zinatengera akulu akulu akhonsolo komanso odziwa zamalamulo kuunika dandauloli ndipo atakambilana mukanyumba kamata, anagwirizana kuti a Nyirenda ndi oyonera kuima chifukwa khoti silinagamule mlanduwu.

Panopa zisankho zikupitilirabe kusankha wachiwiri kwa meya wa mzindawu.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malawi mourns with Namibia — President Chakwera

MBC Online

Government launches Agricultural Diversification, Commercialisation booklet

MBC Online

Mukatengera chipani njala ikusautsani, watero Kalitendere

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.