Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Komiti yakunyumba yamalamulo yakhutira ndikuthetsedwa kwa mlandu wa a Chilima

Mkulu ozenga milandu yaboma, a Masauko Chamkakala

Komiti yakunyumba yamalamulo yoona zamalamulo yati yagwirizana ndi zifukwa zomwe mkulu ozenga milandu yaboma, a Masauko Chamkakala, anaathetsera mlandu wa wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Dr Saulos Chilima.

Iwo ati mlanduwu  umakhudza chitetezo chadziko ndipo sungabwelere kubwalo lamilandu.

Malinga ndi wapampando wakomitiyi, a Peter Dimba, mlandu omwe ubwelere kubwalo lamilandu pakadali pano omwe mkulu ozenga milandu yaboma m’dziko munoyu adaauthetsa ndiokhudza kampani ya Paramount Holdings.

A Dimba ati umboni omwe a Chamkakala anafotokozera komitiyi kuti athetse mlandu okhudza kampaniyi siogwirika.

Akuluakulu a kampani ya Paramount Holdings amkawaimba mlandu opereka zikalata zabodza kuti apeze mwayi operekera katundu ku nthambi komanso maunduna ena aboma, pomwe wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino  amkamuimba mlandu okhudzana ndi katangale.

Related posts

Treasury to sign 2024/25 letters of expectations with Parastatals

Mayeso Chikhadzula

Women farmers in Mwanza brace for new season amid climate change

Romeo Umali

‘Pangani katundu oyenera pa msika wakunja’

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.