Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Boma likuyika maziko a chitukuko — Dr Chakwera

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati boma likuyika maziko okhazikika oti apindulire dziko lino kuyambira panopa mpakana mibadwo yamtsogolo.

Dr Chakwera amayankhula izi pa Kabwinja, kuzambwe kwa boma la Dowa, pamene amalankhula ndi a Malawi.

Iwo anati ngakhale dziko lino lakumana ndi ziphinjo zambiri, makamaka ngozi zogwa mwadzidzi muzaka zinayi zapitazi, zinthu zikuyenda kumbali ya ntchito zomangamanga monga misewu, nyumba za anthu ogwira ntchito ku nthambi zachitetezo ndi sukulu.

Mtsogoleriyu anati boma lionjezera chiwerengero cha opindula ku thandizo la chakudya komanso fetereza ndi mbewu zotsika mtengo kaamba kakuti limamvera zofuna za a Malawi.

Iwo anaonjezeranso kuti misewu ya kumidzi ailambula kuti alimi adzitumiza mbewu ku misika mosavuta.

Mfumu Chakhaza yaderalo inayamika boma chifukwa cha ulimi wa nthilira umene ukuchutika mderalo pa mahekitala 483, komanso chifukwa chofikitsa magetsi ndi netiweki ya lamya za mmanja.

Olemba: Isaac Jali

Related posts

Collaboration key to achieving MW 2063 – Banda

Rabson Kondowe

Anthu a ku Ntcheu ndiwothokoza – Nyakwawa Gwedeza

Alinafe Mlamba

CTS cites customer care as lifeblood of business

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.