Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Bambo agwililira mwana

Apolisi ku Lilongwe amanga a Symon Josephy, 35, powaganizira kuti anagwililira mwana wa zaka zisanu ndi zinayi (9) yemwenso ndi mchemwali wa mkazi wa bamboyo.

Wachiwiri kwa ofalitsa nkhani za polisi ya Lilongwe, a Khumbo Sanyiwa, ati bamboyo anapita komwa mowa kumene anabwerako usiku ndipo atafika anapeza mkazi wake wagona. Kenako anapita kuchipinda komwe amagona mwanayo ndi kumugwililira.

A Sanyiwa anati mkazi wa bamboyo atapita ku chipinda cha mwanayo kuti akamuone, anadabwa kuti mwanayo wagwiliridwa. Atamufunsa, bamboyo anavomera kuti wachita izi ndi iyeyo.

A Josephy amachokera m’mudzi wa Sitenala, mfumu yaikulu Mpemba ku Dedza ndipo akaonekera kubwalo lamilandu posachedwapa pa mlandu ogwililira.

 

Related posts

Ntchito yopanga ziphaso ku Mangochi ikutheka

Alinafe Mlamba

Immigration ikufuna kukhala ya mphamvu pa masewero

Rabson Kondowe

Malawi Hockey Team struggle in Zambezi Test Series opener

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.