Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Bambo agwililira mwana

Apolisi ku Lilongwe amanga a Symon Josephy, 35, powaganizira kuti anagwililira mwana wa zaka zisanu ndi zinayi (9) yemwenso ndi mchemwali wa mkazi wa bamboyo.

Wachiwiri kwa ofalitsa nkhani za polisi ya Lilongwe, a Khumbo Sanyiwa, ati bamboyo anapita komwa mowa kumene anabwerako usiku ndipo atafika anapeza mkazi wake wagona. Kenako anapita kuchipinda komwe amagona mwanayo ndi kumugwililira.

A Sanyiwa anati mkazi wa bamboyo atapita ku chipinda cha mwanayo kuti akamuone, anadabwa kuti mwanayo wagwiliridwa. Atamufunsa, bamboyo anavomera kuti wachita izi ndi iyeyo.

A Josephy amachokera m’mudzi wa Sitenala, mfumu yaikulu Mpemba ku Dedza ndipo akaonekera kubwalo lamilandu posachedwapa pa mlandu ogwililira.

 

Related posts

National Bank of Malawi supports NGOs Day with K4 million

Rabson Kondowe

Achinyamata asamadziyang’anire pansi, watero Belekanyama

Romeo Umali

NGO champions eco-friendly products to combat climate change effects

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.