Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Alimi akonzeke kunyotsolerana K14M’

Banki ya NBS yakhazikitsa mpikisano watsopano wa alimi omwe akuutcha K14 million yonyotsolerana, momwe alimi komanso makasitomala abankiyi adzipata mphotho zosiyanasiyana popikisana kusunga ndalama.

Poyankhula ku Lilongwe pamwambo okhazikitsa mpikisanowu, mkulu owona zamalonda Ku bankiyi, Victoria Chanza, wati mpikisanowu ndimbali imodzi yolimbikitsa mchitidwe osunga ndalama ku banki pakati pa alimi komanso makasitomala ndipo alimi akuyenera kumasunga ndalama kuyambira K500,000 pofuna kulowa nawo.

Mumpikisanowu, omwe ndiwa miyezi itatu, alimi adzipambana mphotho zapamwezi monga mbewu, fertilizer, njinga komanso katundu wina wa bankiyi kupatula ndalama pomwe mmodzi wamphumi adzapate mphotho yaikulu ya K2 million m’mwezi wa September.

 

Olemba: Foster Maulidi

Related posts

Standard Bank Malawi for empowered HR Managers

Romeo Umali

JICA impressed with KIA operations

Romeo Umali

Maranatha yatumiza ana ambiri ku sukulu za ukachenjede

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.