Malawi Broadcasting Corporation
International News

Apolisi amanga munthu amene amafuna kupha Trump

Apolisi m’dziko la America amanga a Vem Miller, 49, powaganizira kuti amafuna kupha mtsogoleri wakale wa dzikolo, a Donald Trump.

Malinga ndi ofalitsankhani wa apolisi kumeneko, a Chad Bianco, oganiziridwayu, yemwe amanamizira kuti ndi mtolankhani, anamugwira akufuna kulowa pa zipata za bwalo la Coachella Valley ku California komwe a Trump amachititsa msonkhano okopa anthu.

Apolisi atafufuza m’galimoto mwa a Miller anapezamo mfuti ziwiri, zipolopolo zochuluka komanso ziphaso zoyendera zachinyengo zomwe zinali ndi mayina a anthu osiyanasiyana.

A Miller akhala munthu wachitatu kumangidwa poganiziridwa kuti amafuna kupha a Trump.

A Trump, omwe ndi achipani chotsutsa cha Republican, ndi mmodzi mwa anthu omwe akupikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wa dzikolo pa zisankho zomwe zichitike mu November chaka chino.

Olemba: Alufisha Fischer

Related posts

Why Malawian players’ foreign moves often end early

Romeo Umali

Govt to launch MCA Land Productivity Project next week

Romeo Umali

Illovo Sugar launches three-day health camp in CK

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.