Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

A Kaliati akufuna kudzapikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wa UTM

Pamene chipani cha UTM chikukonzekera kudzachita msonkhano wake waukulu mwezi wa mawa, mlembi wamkulu wa chipanichi, a Patricia Kaliati, alengeza kuti adzapikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri.

Kudzera pa tsamba lawo la mchezo la Facebook, iwo ati ali ndi ukadaulo pa nkhani za ndale potengera kuti akhala akugwira ntchito m’boma mmaudindo osiyanasiyana kuyambira m’chaka cha 1994 ndipo ali ndi chikhulupiliro kuti atha kukwanitsa kutsogolera chipanichi mosavuta.

Msonkhano waukuluwu udzachitika pa 17 November chaka chino.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Dr Michael Usi, ndiye mtsogoleri wa chipani cha UTM.

 

Olemba: Alufisha Fischer

Related posts

‘Social Cash Transfer Programme will reach vulnerable people’

Romeo Umali

Mia wati adzapikisana nawo pampando wa wachiwiri kwa wachiwiri kwa mtsogoleri ku MCP

Mayeso Chikhadzula

Progress in Human-Wildlife Conflict Reduction Reported by Tourism Ministry

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.