Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Wapha mkazi wake chifukwa cha nsanje

Mwamuna wazaka 42, Isaac Patisi, wakadzipereka ku polisi ya Area 3 ku Lilongwe atapha mkazi wake Azefa Kasamanda wazaka 36 pomukhapa ndi nkhwangwa.

Mneneri wapolisi ku Lilongwe, Hastings Chigalu, wati izi zachitika ku dera la Malingunde m’boma lomwelo la Lilongwe.

Malinga ndi a Chigalu, mwamunayu anakangana ndi mkazi wake usiku pomuganizira kuti ali pa ubwenzi wamseli ndi mwamuna wina.

Mkangangano utakula, Patisi anadzuka ndikutenga nkhwangwa kukhapa mkazi wakeyo pachifuwa iye ndikuthawa.

Kenako mwamunayo anafotokozera mchemwali wa malemuyo zankhaniyi asanakadzipereke kupolisi.

Related posts

GOVT PLEDGES TO SUPPORT CREATIVE INDUSTRY

MBC Online

Ana a m’mudzi bwerani muthandize kwanu – Mfumu Mwamulowe yatero

MBC Online

MZUZU YOUTH CENTRE PROJECT AT 20% COMPLETION RATE

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.