Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

President Chakwera ayamikira ntchito yokonza msewu wa M1

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati ndiokhutira ndi momwe ikuyendera ntchito yokonzanso msewu wa M1.

Dr Chakwera anena zimenezi pa Mtengowanthenga pomwe analankhula kwa nantindi wa anthu amene asonkhana.

Dr Chakwera anati anaganiza  zodutsa mu msewu wa M1 popita ku Mzuzu, kuti awone yekha ntchitoyo.

Iwo anatsimikiziranso anthu kuti ntchito yokonza dzikoli ili mkati, kuti mibadwo ikubwerayi idzakhale ndi dziko labwino, ndipo anayamika anthu aku Dowa chifukwa ndi olimbika pa ntchito.

Mtsogoleri wa dziko linoyu anati nkofunika kuti dziko la Malawi likhale lodzidalira osati lopempha pempha.

“Komanso tiyeni tisamalire ntchito zachitukuko zomwe tili nazo, osaononga ayi ” anatero Dr Chakwera.

 

Olemba: Isaac Jali

Related posts

MALAWI EARNS $65,000 FROM BELL PEPPER EXPORTS TO SOUTH AFRICA

Rabson Kondowe

Chakwera calls for nationwide prayers for missing plane

Romeo Umali

Malawi records 1,700 suicide-related deaths

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.