Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Awanjata pogulitsa mankhwala owopsa

Anthu asanu ndi awiri awatsekera ku polisi ya Ntcheu atawagwira akugulitsa mankhwala owopsa ophera tizilombo monga anankafumbwe mopanda chiloleza m’misika m’bomali.

Mmodzi wa akuluakulu ku bungwe la Pesticides Control Board, a Benson Kaphandira, ati mankhwalawa omwe ndi amapilisi komanso ena amadzi, ndi owopsa kotero kuti akuvulaza komanso kupha anthu ochuluka.

Mneneri wa apolisi ku Ntcheu, a Jacob Khembo, ati anthu  omwe awamangawa, akuyankha milandu yogulitsa mankhwala owopsa popanda chilolezo komanso kugulitsa mankhwala osavomerezeka.

Iwo ati ntchitoyi ipitilira pothana ndi mchitidwewu.

Related posts

Rights groups want new prison law

Rabson Kondowe

Chakwera deserves second term – MCP diaspora wing

Rabson Kondowe

Empower women, girls with disabilities — FEDOMA

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.