Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Wapereka mbatata yophika kuti asamuulure kuti wagwilira ana awiri

A Polisi ku Limbe mu mzinda wa Blantyre anjata a Paul Jalasi azaka 46, powaganizira kuti anagwilirira ana awiri a zaka zisanu ndi zitatu komanso wina wazaka zisanu zokha.

Ofalitsankhani ku Polisiyi, a Aubrey Singanyama, ati a Jalasi anawapatsa anawa mbatata kuti asakaulule pamene adachita mlanduwu ku Bangwe.

A Singanyama ati izi zidachitika pamene amayi a anawa anali kochita malonda ku msika wa Limbe ndipo m’modzi mwa amayiwa anauzidwa za upanduwu ndipo anakamang’ala nkhaniyi ku Polisi kuti bambo amene akumuganizirayu amukwidzinge.

A Jalasi amachoka m’mudzi wa Chingoni kwa mfumu yayikulu Mponda m’boma la Ntcheu.

 

Related posts

Chakudya si nsima yokha – LUANAR

Rabson Kondowe

‘Ntchito ya maphunziro ndi umoyo wabwino m’sukulu ikonzedwenso’

Rabson Kondowe

NRB yalemba anthu opyola 12 million

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.