Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani Sports Sports

Wanderers idzasankha mphunzitsi watsopano gawo loyamba la super league likatha

Timu ya Mighty Mukuru Wanderers yati idzasakha mphunzitsi watsopano gawo loyamba la super league likatha ndipo yati yemwe akugwirizira udindowu Meke Mwase ali ndi mwayi waukulu otengeratu ntchitoyi.

Mwase akuthandizidwa ndi Bob Mpinganjira kutsatira ndipo adatenga udindowu pambuyo pa kutula pansi udindo kwa Nsazurwimo Ramadan.

Mkulu watimuyi, Panganeni Ndovi, wati aunikira mmene aphunzitsi ogwirizirawa agwilira ntchito gawo loyamba likatha.

Motsogozedwa ndi Mwase, timuyi yapambana masewero ake onse awiri.

Wandereres ili panambala yachitatu mu ligi ndi ma pointi 18.

By Praise Majawa

Related posts

Nine Malawians to study in Ireland under Irish Aid

MBC Online

UK grants Malawi about K7BN to help those affected by El Nino

Rabson Kondowe

Malawi will eradicate cholera by 2030 – IFRC

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.