Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani Sports Sports

Wanderers idzasankha mphunzitsi watsopano gawo loyamba la super league likatha

Timu ya Mighty Mukuru Wanderers yati idzasakha mphunzitsi watsopano gawo loyamba la super league likatha ndipo yati yemwe akugwirizira udindowu Meke Mwase ali ndi mwayi waukulu otengeratu ntchitoyi.

Mwase akuthandizidwa ndi Bob Mpinganjira kutsatira ndipo adatenga udindowu pambuyo pa kutula pansi udindo kwa Nsazurwimo Ramadan.

Mkulu watimuyi, Panganeni Ndovi, wati aunikira mmene aphunzitsi ogwirizirawa agwilira ntchito gawo loyamba likatha.

Motsogozedwa ndi Mwase, timuyi yapambana masewero ake onse awiri.

Wandereres ili panambala yachitatu mu ligi ndi ma pointi 18.

By Praise Majawa

Related posts

CHAKWERA, MNANGAGWA ATTEND IAFT 2023

MBC Online

Nsanje DC calls for stakeholder collaboration ahead of 2025 election

Alinafe Mlamba

‘Demanding fees from patients is illegal’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.