Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Prezident Chakwera wafika pa Kaphuka Trading Centre ku Dedza

Mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera, ali kwa mfumu yayikulu Kaphuka ku Dedza pamsonkhano wakalawe m’bomali.

Polankhula kwa anthu ochuluka omwe anasonkhana pa sitolo za pa Kaphuka, Dr Chakwera anati akudziwa bwino za njala imene anthu ali nayo mderali kaamba ka ng’amba yomwe inalipo chaka chatha.

Mtsogoleriyu watsimikizira anthu kuti chakudya chomwe boma layamba kale kugawa chifika posachedwapa kuderali.

Pamenepa, iye analimbikitsa anthuwa kuti asaiwale kukalembetsa mukaundula wa chisankho kuti adzathe kuponya nawo mavoti chaka cha mawa.

Ndipo phungu wadera la Dedza Central East, a Joshua Malango, apempha boma kuti lionjezere thandizo la chakudya kuderali.

Phunguyu wapemphanso anthu mderali kuti apitirize kukalembetsa maina mukaundula wa chisankho kuti adzathe kuvota pa chisankho chaka chamawa.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Thandizo lakulera, uchembere wabwino laphweka ku Phalombe

Beatrice Mwape

10May wayamba kupepesa

Emmanuel Chikonso

MEC, oweruza a Malawi ndi Kenya aombana mitu paza milandu ya chisankho

Emmanuel Chikonso
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.