Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tifikireni nthawi zonse -OPC

Ofesi yoona zofalitsa nkhani mu ofesi ya mlembi wamkulu wa boma ndi nduna OPC yalangiza atolankhani kuti apitirize kugwira  bwino ntchito ndi boma.

Mneneri wa ofesi yi, a Robert Kalindidza ndiomwe anena izi ku Mulanje pamsonkhano waukulu wapa chaka wa atolankhani achikatolika m’dziko muno.

A Kalindidza ati atolankhani amagwira ntchito yayikulu yofalitsa mauthenga  ndi ndikuzindikiritsa anthu kotero ndi bwenzi leni leni la boma pa chitukuko.

Poyankhulapo, wachiwiri kwa wamkulu wa bungweli mayi Josephine Chinele ati bungwe la Association of Catholic Journalists-ACJ lachita zinthu zochuluka pothandidza  pa chitukuko chadziko lino monga kuthandidza  anthu ovutika  munthawi ya ngozi  zogwa  mwadzidzi

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Promise Kamwendo wapepesa!

Romeo Umali

Bushiri apereka chimanga kwa mabanja 200 ku Mangochi

MBC Online

‘Masewero ndi njira yofalitsa uthenga wa uchembere wabwino’

Simeon Boyce
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.