Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tidzayika zipilala, sitinatseke barrage – Water Authority

Bungwe la National Water Resources Authority lati lili ndi mapulani omanga zipilala zomwe zithandize kuletsa anthu kumanga zinthu zosiyanasiyana m’phepete mwanyanja.

Mkulu wabungweli, a Dwight Kambuku, alankhula izi kutsatira kukwera kwa mlingo wamadzi mu nyanja ya Malawi, zomwe zachititsa kuti nyumba ndi zinthu zina zomwe anthu anamanga m’mbali mwanyanjayi zikhale zili mmadzi.

A Kambuku atsindikanso kuti bungwe lawo silinatseke Kamuzu Barrage ku Liwonde monga momwe anthu akhala akunenera kuti kutseka kwa pamalowa  ndikomwe kwachititsa kuti mlingo wamadzi ukwere mnyanja ya Malawi.

“Ndikulakwa kumanena kuti bungwe lathu latseka Kamuzu Barrage popeza, mwa zina, madzi omwe amadutsa pa Kamuzu barrage amawagwiritsa ntchito popanga magetsi komanso Southern Region Water Board ndi Blantyre Water Board amakhala akupopa madziwa ndikugawira anthu,” anatero a Kambuku.

Pofika lachitatu, madzi akuti afika mlingo wa mamita 476.3.

Related posts

MEPA, environmentalists spar on thin plastics ban

MBC Online

Tiyeni tipitirize kumvera mtsogoleri komanso kukonda chipani chathu — Msukwa

Romeo Umali

BAM AGM aims to drive financial inclusion in rural areas

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.