Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Sendeza ayendera Hope Orphanage

Nduna yoona za chisamaliro cha anthu, a Jean Sendeza, lero ikuyendera Hope Orphanage, m’boma la Mchinji kuti imve ena mwa mavuto amene ana komanso akuluakulu oyendetsa malo amenewa akukumananawo.

Pamalowa, pakukhala ana oposera 600, ndipo sapereka ndalama ina iliyonse.

Awa ndi malo amene Madonna, oyimba wa m’dziko la America, anatenga David Banda ndi kukhala mwana wake m’chaka cha 2008.

Pamalowa pali sukulu ya nursery, primary, sekondale komanso yophunzitsa ntchito za manja, monga kusoka, kuwotchelera komanso zomangamanga.

M’busa Thomson John Chipeta anakhazikitsa malowa m’chaka cha 1998.

 

Related posts

Traditional leaders warned against nepotism

Rabson Kondowe

‘Tisalore katangale pa ntchito zaumoyo’

Romeo Umali

Bullets is confident — Pasuwa

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.