Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Politics

President wa Guinea-Bissau akudzapepesa maliro a Dr Chilima ndi ena

Mtsogoleri wa dziko la Guinea-Bissau a Umaro Sissoco Embalo afika m’dziko lino mawa Lachisanu kudzapepesa imfa ya amene wachiwiri kwa m’tsogoleri wa dziko lino Dr Saulos Chilima ndi anthu ena omwe anamwalira pangozi ya ndege yomwe inachitika mu nkharango ya Chikangawa ku Mzimba.

Chikalata chomwe atulutsa amu ofesi yoona nkhani zakunja kwa dziko lino chatsimikiza kuti President Embalo akudzakumana ndi President Dr Lazarus Chakwera.

Mtsogoleriyu akuyembekezeka kudzafika pa bwalo la ndege la Kamuzu International ku Lilongwe mma 10:35 am ndipo adzanyamuka m’dziko muno kubwelera kwawo mawa lomwelo mma 1:30pm.

 

Related posts

NATIONAL PRODUCT MAGAZINE CELEBRATES 100TH EDITION

McDonald Chiwayula

Legislator vows to enhance education standards

Romeo Umali

Senaji in Kenya’s World Cup qualifier squad

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.