Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Entertainment Local Local Music News Nkhani

Oimba aphunzire kugwira ntchito ndi aluso ena — Billy Kaunda

Billy Kaunda walangiza oimba kuti aphunzire kugwira ntchito ndi aluso ena monga alakatuli.
Kaunda wayankhula izi pomwe wati akubwera ndi chimbale chatsopano posachedwapa momwe Okoma Atani Malunga, katswiri pandakatulo, wamulembera nyimbo zingapo.
“Sikoyamba kugwira ntchito ndi a Malunga pankhani yanyimbo, anandipatsapo ndakatulo ya ‘Naliyera’ komanso ‘Mawu Angawa’ mwazina,” anatero Billy Kaunda.
Iye wati pakadalipano akutangwanika ndi ntchito zina monga zakunyumba yamalamulo ngakhale wati zokhudza chimbale chake zilimchimake.

Related posts

RA ilonjeza kukonza misewu ndi milatho

Romeo Umali

Media Council drills journalists on safety during elections

Blessings Kanache

We got you covered — NEEF

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.