Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Oganiziridwa za “Bakili Muluzi TV” akudikira kumva za belo

Bwalo la milandu la Magistrate munzinda wa Lilongwe likuyembekezeka kupereka chigamulo pa pempho la belo la a  Chiyanjano Mbedza, amene akuwaganizira kuti amafalitsa nkhani zabodza patsamba la mchezo  limene amalitcha  Bakili Muluzi TV.

Loya wawo, Gilbert Khonyongwa, ndiye anapereka pempholi  lachitatu sabata ino.

Mulanduwu umayembekezeka kuyamba nthawi ya 9 koloko mmawa uno koma wachedwerapo kaamba koti akudikira oweruza.

Mbedza anamangidwa pa 22 July chaka chino mu mzinda wa Blantyre.

 

Olemba ndi ojambula: Emmanuel Chikonso ndi Thokozani Jumpha

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Police to deploy intelligence-driven operation

Chisomo Break

M’mbelwa DC develops bursary provision tool

Beatrice Mwape

NICO seeks to revive Zambian subsidiary

Earlene Chimoyo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.