Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Ntchito yomanga misewu ikuyenda bwino ku Lilongwe’

Ena mwa anthu amene amagwiritsa ntchito misewu ya mu mnzinda wa Lilongwe ati ndi okondwa ndi mmene ntchito yomanga misewu mu mnzindawu ikuyendera.

Poyankhula ndi MBC, a Biliati Basikolo amene amayendetsa minibus yoyenda ku Area 25 kupita mu tauni ya Lilongwe ati ndi wokondwa kuona momwe roundabout ya Amina yasinthira mu kanthawi kochepa munzindawu.

“Tikamayenda pena kumaona ngati tili kunja kwa dziko lino. Misewu yake ikukhala yapamwamba,” anatelo a Basikolo.

Malinga ndi malipoti, misewu imene ikumangidwa monga wa Mzimba Street, Kanengo-Crossroads ndi Kenyatta Drive ikhoza kutha mwachangu poyerekeza ndi mmene oyendetsa ntchitoyi amaganizira poyamba.

Mseu wa Kanengo-Crossroads akumanga  ndi a kampani ya Shadong Liquao ya mdziko la China ndi thandizo la ndalama zoposa K22 billion.

Msewu wa Mzimba Street akumanga ndi a kampani ya Mota Engil.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

‘A Chakwera ataya kholo mu uzimu’

Beatrice Mwape

TAMA Farmers Trust yayamikira boma pa mitengo yabwino ya fodya

Mayeso Chikhadzula

‘Apatseni chisamaliro chabwino ana’

Olive Phiri
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.