Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Nkhani

Ntchito yomanga malo opereka madzi ku Mangochi yafika theka – SWRB

Bungwe loona za madzi la Southern Region Water Board (SWRB) lati  ntchito yomanga malo omwe adzipereka madzi kwa anthu okhala mmadera ozungulira Makanjira ku Mangochi tsopano yafika theka, kuchokera pomwe ntchitoyi inayamba mwezi wa July chaka chino.

Mkulu wa bungweli, a Duncan Chambamba, anena izi pamene komiti ya aphungu akunyumba ya Malamulo yoona za chilengedwe imayendera  ntchito yomanga malowa yomwe akuitcha  Makanjira Water Supply Project.

Malinga ndi bungweli, zina mwa ntchito zomwe zikugwilika pamalowa, ndikuika ma pipe omwe adzithandizira kupopa madzi kuchokera pa nyanja ya Malawi, kumanga malo osungila ndi kusamalira madzi asanapite mmipope komanso kumanga nyumba za ogwira ntchito.

Wapampando wa komiti ya aphungu akunyumba ya malamulo yoona za chilengedwe, a Welani Chilenga, ati komitiyi ndi yokhutila ndi momwe ntchito yachitukuko cha madzi  ikuyendera pa malowa.

“Tadzionera tokha kuti ntchitoyi ikuyenda bwino koma kontalakitala wadandaula kuti kuchedwa kwa malipilo ndi limodzi mwa mavuto omwe akukumana nawo ndiye nkhani imeneyi tikaitula mmanja mwa unduna wa zachuma,”Atero a Chilenga.

Anthu pafupifupi 68,000 ndiomwe akuyembekezeka kupindula popeza madzi abwino m’derali, ntchitoyi ikatha pofika mwezi wa July chaka cha mawa.

 

Olemba Owen Mavula

Related posts

President Chakwera to open Agriculture Investment Conference

Romeo Umali

Ayamikira Chitukuko cha milatho

Rabson Kondowe

Police IG urges officers to rebuild public trust, tackle mob justice

Yamikani Simtowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.