Malawi Broadcasting Corporation
International News Nkhani

‘Nduna yayikulu ku UK idzigula yokha zovala, magalasi a maso’

Nyumba yowulutsa mawu ya BBC yati nduna yaikulu ya m’dziko la United Kingdom, a Sir Keir Starmer, asiya kulandira thandizo la ndalama zoti adzigulira zovala komanso magalasi a m’maso zoti adzivala akamapita ku ntchito.

Nzika za dzikolo zakhala zikudzudzula ndunayi, maka zitadziwikanso kuti a chipani cha Labour, kudzera mwa a Waheed Ali, anawapatsa a Starmer £16,000 yomwe ndipafupifupi K37 million.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wakale wa chipanichi, a Baroness Harman, anati ndi odabwa ndi izi chifukwa munthu aliyense amayenera azizigulira yekha zovala zoti adzivala akamapita ku ntchito.

Mbuyomu, a Starmer akhala akudzudzulidwanso zitadziwika kuti akhala akulandira ma tiketi a ndalama zankhaninkhani oti adzigwiritsa ntchito akafuna kukaonera mpira ulionse wa timu ya mpira wa miyendo ya Arsenal.

Olemba: Alufisha Fischer

Related posts

Kafukufuku akuti chikhulupiliro mwa aphungu ndi makhansala chikuchepa

Alinafe Mlamba

Athana ndi umphawi pokonza sopo

Romeo Umali

David versus Goliath affair in Airtel Top 8’s eighth season opener

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.