Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Ndege imene anakwera a Chilima yasowa

Asilikali ankhondo, mothandizana ndi nthambi zina zaboma, ali mkati mofufuza kuti apeze kumene kuli ndege imene inanyamula wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Dr Saulos Chilima.

Malinga ndi kalata imene wasayinira ndi mlembi wamkulu mu ofesi ya prezidenti ndi nduna zake, a Colleen Zamba, ndegeyo, imene ndiya MDF, imayembekezeka kutera mma 10:02 kummwawa munzinda wa Mzuzu kuchokera ku Lilongwe koma akuti inasowa pa makina amene amaonerapo ndege ndipo siidaonekenso.

A Zamba ati potsatira izi, mkulu wa asilikali ankhondo m’dziko muno, a Valentino Phiri adziwitsa mtsogoleri wadziko lino Dr Lazarus Chakwera, amene wayimika ulendo wake umene amayenera kunyamuka lero kupita ku Bahamas.

Mtsogoleri wadziko linoyu ndiye walamulanso asilikali ndi ena kuti ayambe kusakasaka ndegeyo.

Malipoti akusonyeza kuti a Chilima amayembekezeka kukakhala nawo pamwambo oyika m’manda a Raphael Kasambara,umene wachitika m’boma Nkhata Bay.

Related posts

Bungwe la CARD lati MBC ndi akadaulo powulutsa mawu

Romeo Umali

Malawi commends UNDP’s support towards digital transformation

Mayeso Chikhadzula

Artists withdraw from 2024 Maso Awards over voting concerns

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.