Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MWASIP ilimbikitsa kalembera wa malo

Unduna wa zamalo wati wakwanitsa kulembera malo oposa 50,000 mukaundula wamalo a umwinimwini, pansi pa ntchito ya chitukuko cha Malawi Watershed Services Improvement Project (MWASIP) ku Chingale m’boma la Zomba.

Mmodzi wa akuluakulu mu undunawu, a Anthony Nzima, anena izi pamkumano umene anali nawo ndi olembankhani munzinda wa Blantyre.

Malinga ndi akuluakulu achitukuko cha MWASIP, ntchito yakalembera wa malo, mwazina, ikuchitika ndicholinga chofuna kubwezeretsa zachilengedwe komanso kuteteza nthaka.

Pakadali pano, a Nzima ati ntchitoyi ili mkati m’maboma a Blantyre ndi Machinga atatsiriza m’boma la Zomba.

 

Olemba: Simeon Shumba

Related posts

Inclusive social protection crucial for persons with disabilities

Blessings Kanache

Dedza North West MP boosts village savings groups

Romeo Umali

Achievement of Malawi 2063 at stake if women are neglected — NICE

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.