Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MWASIP ilimbikitsa kalembera wa malo

Unduna wa zamalo wati wakwanitsa kulembera malo oposa 50,000 mukaundula wamalo a umwinimwini, pansi pa ntchito ya chitukuko cha Malawi Watershed Services Improvement Project (MWASIP) ku Chingale m’boma la Zomba.

Mmodzi wa akuluakulu mu undunawu, a Anthony Nzima, anena izi pamkumano umene anali nawo ndi olembankhani munzinda wa Blantyre.

Malinga ndi akuluakulu achitukuko cha MWASIP, ntchito yakalembera wa malo, mwazina, ikuchitika ndicholinga chofuna kubwezeretsa zachilengedwe komanso kuteteza nthaka.

Pakadali pano, a Nzima ati ntchitoyi ili mkati m’maboma a Blantyre ndi Machinga atatsiriza m’boma la Zomba.

 

Olemba: Simeon Shumba

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Embrace change – Director of Agriculture

MBC Online

IMF HAPPY WITH STRIDES TO REVIVE ECONOMY

MBC Online

Boy in cooler for murder

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.