Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Local Local News Nkhani

Mutharika wati aMalawi adzilima mbewu zopilira ng’amba

Mtsogoleri wakale wadziko lino, Professor Peter Mutharika, wapempha anthu m’dziko muno kuti adzitenga mbewu zina ngati chakudya mmalo momangodalira nsima.

A Mutharika anena izi pa mwambo wachaka chino wa Mulhako wa Alhomwe omwe umachitikira ku likulu la Alhomwe kwa Chonde m’boma la Mulanje.

Iwo anati makolo akale ankadalira mbewu za mapira, chinangwa ndi mbatata, mwa zina, ngati chakudya ndipo samakhala ndi njala kwambiri. Iwo anaonjezeranso kuti mbewuzu sizifuna mvula yambiri, zimene zili zogwirizana ndi momwe mvula ikumagwera masiku ano.

Pamwambowu, mtsogoleri wakaleyu anapemphanso achinyamata kuti adzilimbikira maphunziro chifukwa angawathandize ku khala ndi tsogolo labwino ndiponso anapempha anthu m’dziko muno kuti adzilemekeza achikulire.

Chaka chino, mwambowu umachitikira pamutu wakuti “Mgwirizano wa cholinga chimodzi”.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

NCST sets high expectations on Academy of Sciences

Madalitso Mhango

2 MORE NETTED IN TADIKILA CASE

MBC Online

MACRA to combat hacking, fraud through new campaign

Emmanuel Chikonso
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.