Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani

Munthu mmodzi wavulala modetsa nkhawa pa ngozi ya sitima

Munthu mmodzi wavulala modetsa nkhawa pa ngozi ya sitima ku Blantyre mu njanji ya Magalasi – Nyambadwe – kudutsa ku Chapima.

Ofalitsankhani za polisi ya Ndirande, a Maxwell Jailosi, ati adakafufuzabe za nkhaniyi ndipo a kampani ya CEAR, omwe ndi eni sitimayi, sanapezeke kuti ayankhulepo pa nkhaniyi.

Koma malinga ndi anthu amene akuti anawona ngoziyi ikuchitika, munthuyu anadumpha mu sitimayi, yomwe inali ikuyenda, pamene ena akuti amayesera kukwera sitimayi ikuyenda.

Munthuyu akulandira thandizo la mankhwala pa chipatala cha QECH.

Olemba: Blessings Cheleuka

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Humission steps up environmental conservation efforts

Foster Maulidi

Shuga wafika wambiri pa msika – Kunkuyu

The Harps ikondwerera zaka khumi zamaimbidwe ndi makwaya aku Zimbabwe ndi Zambia

Emmanuel Chikonso
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.