Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani Religion

Atsogoleri azipembedzo alimbikitsa bata

Bungwe la atsogoleri azipembedzo zosiyanasiyana m’dziko muno la Religious Leaders Organisation lapempha anthu kuti adzikhala mwabata nthawi zonse ndi kulemekeza atsogoleri adziko.

Mtsogoleri wabungweli, Sheikh Muhammad Chindamba, walankhula izi ku Lilongwe pamsonkhano omwe anakonza opemphelera dziko komanso kusankha adindo a abungweli.

Iwo ati ndizomvetsa chisoni kuti atsogoleri azipembedzo ena, omwe ntchito yawo ndikukhazikitsa bata ndi mtendere, akumayankhula mobweretsa chisokonezo, maka pamasamba a mchezo.

Iwo ati ndikofunika mtsogoleri wachipembedzo aliyense awonetsetse kuti akulimbikitsa umodzi ndi mtendere.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MBS trains journalists on quality standards reporting

MBC Online

Wirima hails programme transforming schools

MBC Online

Chakwera to officiate private sector agriculture mechanisation

Blessings Kanache
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.