Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

MPONDA NDI MPHUNZITSI WA SILVER STRIKERS

Timu ya Silver Strikers yalemba ntchito Peter Mponda ngati mphunzitsi wa timuyi amene akulowa m’malo mwa Pieter De Jongh yemwe adatula pansi udindo wake mwezi wathawu.

A Mponda awapatsa kontarakiti ya chaka chimodzi komanso awapatsa ufulu osankha mphunzitsi owathandiza.

Mkulu oyendetsa ntchito ku timuyi, a Patrick Chimimba, ndi amene atsimikiza za nkhaniyi pomwe amalandila mphunzitsiyu pa bwalo la ndege la Kamuzu mu mzinda wa Lilongwe Lamulungu masana.

Poyankhulapo, a Mponda anapempha otsatira timuyi kuti akhulupilire ntchito imene agwire posatengera za mbiri yakale.

Mphunzitsi-yu, watsogolerako ma timu monga Premier Bet Wizards, analinso wa chiwiri kwa mphunzitsi wa timu ya Bullets, komanso chaposachedwapa anali akuphunzitsa timu ya Black Leopards ya m’dziko la South Africa.

Olemba: Foster Maulidi.

#mbconlineservices

Related posts

MAYOR’S TROPHY UNEARTH HIDDEN TALENT

Romeo Umali

Sing’anga akakhala kundende pamlandu ogwililira

Rabson Kondowe

First Lady urges new NAM leadership to unearth talent

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.