Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

Mlembi wamkulu wa Synodi akhetsa msozi ku msonkhano waukulu

Msonkhano waukulu wa mpingo wa CCAP mu Sinodi ya Livingstonia anayamba awuyimitsa kaye moderator watsopano wa sinodiyi, m’busa Jairos Kamisa, atadzudzula akuluakulu a mpingowo ‘chifukwa chosokoneza zinthu’.

Iwo anadzudzula akuluakuluwo, kuphatikizapo mlembi wamkulu wa sinodiyi, m’busa William Tembo, kuti amalowelera mu nkhani zandale, komanso amayambitsa zinthu zogawanitsa mpingo ndikuchita ziganizo mosafunsa maganizo a Moderator.

Izi zinachititsa kuti m’busa Tembo akhetse misozi pamaso pagulu lonse limene linasonkhana mu tchalichi cha Embangweni ku Mzimba.

Mmodzi mwa akuluakulu opuma a mpingowo, m’busa Mezuwa Banda, anapempha moderator watsopanoyo kuti zokambiranazo aziyimitse kaye.

Olemba: Hassan Phiri

Related posts

Stakeholders urged to prioritise youth led Initiatives

McDonald Chiwayula

Australia pledges continued support to Malawi

Romeo Umali

Titolera ndalama zokwana K2.18 trillion chaka cha 2023/24 — MRA

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.