Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Religion

Mlembi wamkulu wa Synodi akhetsa msozi ku msonkhano waukulu

Msonkhano waukulu wa mpingo wa CCAP mu Sinodi ya Livingstonia anayamba awuyimitsa kaye moderator watsopano wa sinodiyi, m’busa Jairos Kamisa, atadzudzula akuluakulu a mpingowo ‘chifukwa chosokoneza zinthu’.

Iwo anadzudzula akuluakuluwo, kuphatikizapo mlembi wamkulu wa sinodiyi, m’busa William Tembo, kuti amalowelera mu nkhani zandale, komanso amayambitsa zinthu zogawanitsa mpingo ndikuchita ziganizo mosafunsa maganizo a Moderator.

Izi zinachititsa kuti m’busa Tembo akhetse misozi pamaso pagulu lonse limene linasonkhana mu tchalichi cha Embangweni ku Mzimba.

Mmodzi mwa akuluakulu opuma a mpingowo, m’busa Mezuwa Banda, anapempha moderator watsopanoyo kuti zokambiranazo aziyimitse kaye.

Olemba: Hassan Phiri

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Phungu wa DPP wayamikira boma chifukwa chosakondera

Charles Pensulo

Malawi will face South Africa in COSAFA Beach Soccer opener

Romeo Umali

Apolisi ku Mangochi amanga Boika atam’peza ndi chida choopsya

Davie Umar
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.