Bungwe loyendetsa zisankho m’dziko muno la Malawi Electoral Commission (MEC) yalengeza zotsatira za chisankho cha komiti yaikulu ya chipani cha Democratic Progressive.
A Joseph Mwanamvekha agonjetsa a George Chaponda ndi kukhala wachiwiri kwa mtsogoleri wa chipanichi m’chigawo cha kum’mwera.
A Bright Msaka awasankha kukhala wachiwiri kwa mtsogoleri wa DPP mchigawo cha kum’mawa.
A Alfred Gangata apambana ndikukhala wachiwiri kwa prezidenti wa chipani cha DPP m’chigawo chapakati atapikisana ndi a Paul Gadama.
A Jappie Mhango alowa opanda opikisana naye kukhala wachiwiri kwa mtsogoleri wachipani cha DPP m’chigawo cha kumpoto.
Pa udindo wa mlembi wamkulu wa DPP, a Peter Mukhito agonjetsa a Clement Mwale.
Pa udindo wa mkulu okonza za zochitikachitika m’chipanichi (National Organising Secretary), a Sameer Suleman agonjetsa a Chimwemwe Chipungu.
Pa udindo wa Director of operations a Charles Mchacha ndiwo apambana.
Ndipo mkulu owona zamalamulo mu chipanichi, a Chipiliro Mpinganjira agonjetsa a Charles Mhango.
A Mary Navicha ndiwo asankhidwa pa udindo wa mkulu owona za amayi.
A Gladys Ganda, asankhidwa pa udindo wa mkulu owona zachisankho.
Pa mpando wa mkulu owona za achinyamata, a Norman Chisale awasankha atagonjetsa anthu ena atatu.
A Ben Phiri asankhidwa kukhala mkulu owona za ndale mchipanichi (Director of Political Affairs.)
Pa udindo wa mkulu owona zachuma pali a Ralph Juma omwe agonjetsa a Malison Ndau.
Ndipo a Timothy Khoviwa alowa pa udindo woona zachipemvedzo ( Director of Religious Affairs) popanda opikisana nawo.
A Fyness Mwagonjwa awasankha kukhala paudindo wazosamalira anthu (Director of Social Services) atagonjetsa amai ena atatu.
Awa ndi maudindo akuluakulu ndipo palinso ma udindo ena omwe a MEC alengeza kale.

