Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MBC yati Kapusa anali katakwe

Mkulu wa MBC a George Kasakula ati malemu Geoffrey Kapusa anali munthu yemwe anali katakwe pantchito youlutsa mawu pa kanema komanso kuongolera tsogolo lankhani zoulutsa mawu pakanema m’dziko muno.

A Kasakula anena izi pamwambo oika m’manda a Kapusa, umene uli mkati kumudzi kwawo kwa malemwuwa.

Naye phungu wadera lakummwera kwa boma la Machinga, a Grant Ndecha, anati derali linali lokondwa kaamba kakuti linali ndi munthu yemwe achinyamata amadalira powalimbikitsa pa maphunziro kuti nawo adzakhale ndi ntchito yapamwamba.

MBC yakhala ikuthandiza a Kapusa kuyambira akudwala kufikira pano.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

MW, MOZ JOINT TASKFORCE TO INVESTIGATE TRUCK DRIVER ASSAULT CASE

McDonald Chiwayula

Likoma residents for expedited jetty completion

MBC Online

Mbali ina ya msewu wa Chiwembe sanamange bwino — Chimwendo Banda

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.