Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MBC yati Kapusa anali katakwe

Mkulu wa MBC a George Kasakula ati malemu Geoffrey Kapusa anali munthu yemwe anali katakwe pantchito youlutsa mawu pa kanema komanso kuongolera tsogolo lankhani zoulutsa mawu pakanema m’dziko muno.

A Kasakula anena izi pamwambo oika m’manda a Kapusa, umene uli mkati kumudzi kwawo kwa malemwuwa.

Naye phungu wadera lakummwera kwa boma la Machinga, a Grant Ndecha, anati derali linali lokondwa kaamba kakuti linali ndi munthu yemwe achinyamata amadalira powalimbikitsa pa maphunziro kuti nawo adzakhale ndi ntchito yapamwamba.

MBC yakhala ikuthandiza a Kapusa kuyambira akudwala kufikira pano.

Related posts

Lilongwe Dairy eases hospital bedding shortage with blanket donation

Rabson Kondowe

Mkazi wa malemu Professor Mumba amupeza wolakwa pa mlandu wokupha

Mayeso Chikhadzula

Malawi, others in joint football tournament

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.