Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Entertainment Local Local News Nkhani

Mikozi ibweranso, eni ake atero

Mwini watsamba la mchezo la Mikozi, a Bright ‘Excess’ Chiligo, watsutsa mphekesera zimene zikumveka kuti tsamba lake anthu alichita chiwembu kuti lisowe pa makina a internet.

Chiligo wati tsambali libweleranso Lachisanu chifukwa pali ntchito imene akugwira yopanga tsambali kukhala lotetezeka kwa anthu achinyengo.

“Tawona kuti pa internet pachuluka masamba a mchezo amene akubera dzina lathu la Mikozi ndipo akumayika zinthu zoyipa,” iye anatero.

Anawonjezeranso kuti zimenezi zapangitsa kuti azilandira madandaulo ochuluka kuchokera kwa anthu.

 

Related posts

Court bars Kamangila from posting about Judge Manda on social media

Rabson Kondowe

Silver Strikers to face Mighty Wanderers

Romeo Umali

First Lady’s Shaping the Future Foundation Hosts Fundraising Dinner at Kamuzu Palace

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.